Malawi wanga

Malawi wanga Bad news travels at the speed of light; good news travels like molasses.
(1)

22/07/2024



Bwalo la milandu ku Limbe mu mzinda wa Blantyre lalamula Foster Mathewe Saidi wa zaka 25 kuti akhale kundende zaka 18 kaamba kogwililira msungwana wa zaka 6.

Bwaloli linamvetsedwa kuti mkuluyu pa 21 mwezi watha cha mma 8 koloko usiku adaitana mwanayu yemwe ankadya nsima pa nthawiyo kuti akamugaile ndiwo, koma mwanayo chongolowa m'nyumba mwa mkuluyu, iye adamugwililira.

Koma makolo amwanayu adadabwa kumuona momwe amayendera ndipo atamufunsa iye afotokoza zomwe zidamuchitikira ndipo makolowa adakatula nkhaniyi ku polisi.

Atawonekera ku bwalo la milandu mkuluyu adavomera kulakwa kwake ndipo adapempha bwalo kuti limupatse chilango chofewerapo koma mbali ya boma inati mkuluyu akuyenera chilango chokhwima kuti ena atangerepo phunziro.

Apa ndi pomwe Senior Resident Magistrate Ackia Mwanyongo adati mkuluyu ,yemwe ndi wa m'mudzi mwa Mkawela mfumu yaikulu Inkosi Bvumbwe ku Thyolo, akakhale ku ndende zaka 18 ndi kukagwira ntchito ya kalavula gaga.

Yemwe waonetsa chidwi kudzapikisana nawo pampando wa mtsogoleri wa dziko lino pa chisankho cha chaka cha mawa, Milward T...
22/07/2024

Yemwe waonetsa chidwi kudzapikisana nawo pampando wa mtsogoleri wa dziko lino pa chisankho cha chaka cha mawa, Milward Tobias, wabwereza kuti dziko lino likufunika mtsogoleri yemwe alibe chipani.

Iye wayankhula izi pamene dziko lino lakhala ndi miyezi khumi ndi itatu komanso masiku 25 kuti likhale ndi chisankho chapatatu.

Tobias, kudzera patsamba lake la m’chezo la Facebook, wati ubwino wokhala ndi mtsogoleri wotero mwa zina kumapereka mpata kwa mtsogoleri kugwira ntchito mwa ukadaulo, kumachotsa ndale pakayendetsedwe ka ntchito zaboma komanso munthu aliyense amakhala ndi mwayi wofanana kupeza mwayi m’boma komanso zina.

“Zidzakhala zapafupi kuyanjanitsa fuko la Malawi pakuti sipadzakhala chigawo kapena mtundu omadzimva kuti mtsogoleri ndi wawo,” iye wawonjezera motero.

Kodi mwaonera kale inuyo Jay Jay Cee Mw ft ELI Njuchi - Awa
22/07/2024

Kodi mwaonera kale inuyo Jay Jay Cee Mw
ft ELI Njuchi - Awa

Dzaomboleni galimoto zanu, atero a MRABungwe lotolera misonkho la Malawi Revenue Authority (MRA) lalangiza anthu amene a...
22/07/2024

Dzaomboleni galimoto zanu, atero a MRA

Bungwe lotolera misonkho la Malawi Revenue Authority (MRA) lalangiza anthu amene ali ndi galimoto zawo pachipata cha Songwe Border Post kuti akaombole galimotozi ati chifukwa chakuti zikutha malo pamalowa.

Mmodzi wa akuluakulu ku bungweli, a Steven Kapoloma, ati pamalowa pali galimoto zambiri.

"Anthu ambiri anagula galimoto kunja ndipo zitafika akulephera kuwombola, zomwe zikuchititsa kuti malo ano adzadze galimotozi," a Kapoloma anafotokoza.

Iwo anapempha anthu kuti adzifufuza bwino bwino patsamba lawo ndikuwerengera ndalama zimene zikufunikira kuti awombole galimoto yawo asanayitanitse.

A Kapoloma alangiza anthu kuti atengere mwayi wadongosolo loti akhoza kumalipira ndalama zowombolerazi pang'onopang'ono akangoyitanitsa kuti asamapanikizike.

22/07/2024



MAYI WAMANGIDWA POGONA NDI MNYAMATA WACHICHEPERE

A polisi ku Neno amanga mayi Alice Masamba a zaka 38 powaganizira kuti adagona ndi mnyamata wa zaka 13.

Mneneli wa polisi ya Neno Constable Rebecca Msoliza wati mayiyu usiku wa pa 24 June adaitanira mnyamatayu ku nyumba kwake.

Iwo ati mnyamatayu atafika mayiyu adamuuza mwanayu kuti avule uku naye akuvula zovala, kenako n'kugona naye.

Zitathatu izi mwanayu adayamba kutuluka magazi ku maliseche kwake zomwe zidapangitsa kuti akauze mayi ake.

Koma nkhaniyi siidakatulidwe ku polisi ati kaamba koti anthuwa adakambirana poti ndi pachibale.

Koma patapita masiku zidapezeka kuti mwanayu akuvutikabe maka kumva ululu akamakodza, ndipo apa ndi pomwe nkhaniyi adaikaitula ku polisi omwe amanga mayiyu.

Alice Masamba, yemwe ndi wa m'mudzi mwa Chatenga mfumu yaikulu Mlauli ku Neno, akaonekera ku bwalo la milandu komwe akayankhe mlandu ogona ndi mwana.

Mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera wanenetsa za kufunika komanga zithu zolimba komanso zodalirika kuti anthu adzi...
22/07/2024

Mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera wanenetsa za kufunika komanga zithu zolimba komanso zodalirika kuti anthu adzigwiritsa ntchito kwa nthawi yayitali.

Chakwera wanena izi ler pamene amatsegulira msewu wa Cape Maclear m’boma la Mangochi omwe ndiwautali makilomita 6.

Mtsogoleri wadziko linoyu watsindika kuti msewuwu uthandiza kwambiri alendo komanso anthu okhala ku Cape Maclear omwe akhala akukumana ndi mavuto amayendedwe.

Pakadali pano, Chakwera walimbikitsa anthu kuti adzalembetse mwaunyinji mukaundula wa bungwe lazisankho cholinga kuti adzathe kukaponyera voti boma lake pazisankho za chaka cha mawa.

  Nyamata wina walira mokweza ku lilongwe ndi online business iye amagura Playstation 5 kuchoka ku zomba ndipo anamutumi...
22/07/2024



Nyamata wina walira mokweza ku lilongwe ndi online business iye amagura Playstation 5 kuchoka ku zomba ndipo anamutumizira cartoon yomwe mukuionai muli miyala iwili yomwe analipira 200,000 ngati deposit

Abiti Najere agonekedwa ku chipatala cha Queens ku BlantyreAbiti Najere anagonekedwa ku chipatala cha gulupu cha Queen E...
22/07/2024

Abiti Najere agonekedwa ku chipatala cha Queens ku Blantyre

Abiti Najere anagonekedwa ku chipatala cha gulupu cha Queen Elizabeth, Lachinayi sabata latha atawapeza ndi Malungo aakulu.

Zegede yemwe ndi manager wa Najere wauza Malawi24 kuti padakali pano zinthu zikuoneka kuti zasintha kusiyana ndi m'mene zinaliri.

"Tithokoze Mulungu a Najere akupezako bwino pano ndipo ngati zonse zingakhale mchimake akhoza kutuluka madzulo a lero," iye anatero.

Anafotokozanso kuti Najere anayamba kudwala pa 5 mwezi uno.

Kawiri konse tsopano anthu osadziwika akhala akugumula manda womwe munaikidwa thupi la Madalitso Kasimbwe yemwe adali nd...
22/07/2024

Kawiri konse tsopano anthu osadziwika akhala akugumula manda womwe munaikidwa thupi la Madalitso Kasimbwe yemwe adali ndi nkhungu la chialubino.

Adayeserapo mu 2018 ndipo zinachitikanso usiku wa lachisanu lapitali pa mtumbirawo womwe uli m'mudzi mwa Chinomba kwa mfumu Chikumbu m'boma la Mulanje, koma alepheranso chifukwa akubanja adawawaka mandawa molimba kambiri.

Kasimbwe anamwalira ali ndi zaka 25 mu 2006 atadwala kwa nthawi yaitali.

Mneneri wa polisi ya m'bomali, Innocent Moses, wati akusakasaka anthu omwe achita izi.

A Moses ati ana ena am'mudzi mwa Sakhama anapita ku munda kwawo woyandikana ndi mandawo loweruka ndipo anaona kuti chilizacho chagumulidwa. Anadziwitsa akuluakulu omwe anatsina khutu apolisi.

“Tinathamangira ku mandako n'kupezadi kuti panafukulidwa koma sanafikire bokosi ndipo tinatsimikizanso kuti mtembowo uli m'chimake. Tinabwezeretsa zovutazo n'kukwiriranso molimbitsa," anafotokoza motero a Moses.

Apolisi akulangiza anthu m'bomali kuti apewe khalidweli ndi kuwathandiza kupeza anthu aupanduwa.

short story😂Azibambo kusamala mwana sichinthu chophweka
21/07/2024

short story😂
Azibambo kusamala mwana sichinthu chophweka

Anthu mwafika apa 😂🇲🇼
21/07/2024

Anthu mwafika apa 😂🇲🇼

Biden saimansoMtsogoleri wa dziko la America, Joe Biden, wabwera poyera kuti sadzapikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri ...
21/07/2024

Biden saimanso

Mtsogoleri wa dziko la America, Joe Biden, wabwera poyera kuti sadzapikisana nawo pa udindo wa mtsogoleri wadziko-lo.

Biden wanena izi muchikalata ndipo wati zambiri akhale akuyankhula mtsogolomu.

Komabe kwakukulu, iye wayamikira anthu adziko la America kamba kokhala mtsogoleri wawo.

Biden watinso chidwi chake chikhale kumalizitsa nthawi yomwe wakhala nayo basi.

Ganizoli likhudza pomwe otsatira chipani cha ma Democrats, kuphatikizapo mtsogoleri wa kale wa dziko lo, Barrack Obama, akhala akulangiza a Biden kuti asithe ganizo lawo lodzapikisana nawo pa chisankho cha mtsogoleri wa dzikolo, ponena kuti mwayi odzapambana unali ochepa kwambiri.

Dziko la America likhale ndi chisankho mwezi wa November.

Wolemba: Johans Mumba
Source Al Jazeera

Anthu okhala ku area 23 ku Lilongwe ndi madera ena ozungulira monga Majiga, Kaliyeka, Kawale ndi Chilinde komanso ena ak...
21/07/2024

Anthu okhala ku area 23 ku Lilongwe ndi madera ena ozungulira monga Majiga, Kaliyeka, Kawale ndi Chilinde komanso ena akudandaula kuwanda kwa Nsikizi.

"Sitikugona, tikuyesera kupopera mankhwala koma ayi ndithu sizikusintha kwenikweni," watero Ousman Kambanje yemwe wakhuzikanso ndi mlili-wu ku Majiga.

Tizilombo ta Nsikizi nditating'ono m'maonekedwe, muyeso wake ndi ngati mwina nthangala ya apozi, imakonda kubisala muzinthu zopangidwa ndimatabwa, m'ming'alu mwa khoma, mu zovala ingakhale ndi malo ena ambiri.

Precious Kaogo, yemwe ndi telala mu msika wa Kaliyeka wati ma kasitomala ake akumadandaula chifukwa akasiya zovala kuti asoke pozatenga zikumakhala zanyamula tizilomboti zomwe zikumuonongera malonda ake.

Nsikidzi ikaluma pakhungu pa mayabwa modetsa nkhawa moti ena mpaka pamatupa.

Malingana ndi Richard Mvula mkulu owona za umoyo mu mzinda wa Lilongwe, Nsikizi zilibe kuthekera kopereka mavuto odetsa nkhawa pa thupi la munthu koma chabe zimasowetsa mtendere.

"Mbali yayikulu Nsikizi zimapezeka pakhomo pamunthu chifukwa chosowekera ukhondo," anatsindika a Mvula.

Ma lipoti akusonyeza kuti mu chaka cha 2004, munthu wina anapeza Nsikizi pa mpando omwe anakhala mu ndege yochokera ku America kupita ku Canada.

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr. Lazarus Chakwera, mawa agwira ntchito zosiyanasiyana m’boma la Mangochi. Amu ofesi ya prez...
21/07/2024

Mtsogoleri wa dziko lino, Dr. Lazarus Chakwera, mawa agwira ntchito zosiyanasiyana m’boma la Mangochi.

Amu ofesi ya prezidenti ndi nduna ati poyamba, Dr Chakwera ayendera esiteti ya Chitakale kudera la Senior Chief Bwananyambi m’boma la Mangochi.

Kenako mtsogoleriyu akayendera ntchito yomanga ofesi zapa khonsolo ya Mangochi m’dera la Senior Chief Mponda ndipo adzamaliza ndikuyendera ntchito yomanga msewu wa Monkey Bay - Cape Maclear kudera la Senior Chief Namkumba m’bomali.

A mu ofesiyi ati Dr Chakwera akayamba kuyendera ntchitozi nthawi ya 9 koloko mmawa.

Chi family chobebah 😍💟
21/07/2024

Chi family chobebah 😍💟

Ndine Prezidenti wa UTM - Dr UsiWachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Dr Michael Usi, wati malinga ndi malamulo oyendet...
21/07/2024

Ndine Prezidenti wa UTM - Dr Usi

Wachiwiri kwa mtsogoleri wadziko lino, Dr Michael Usi, wati malinga ndi malamulo oyendetsera chipani cha UTM, pakali pano iwo ndi mtsogoleri wa chipanichi.

Dr Usi anena izi pa msonkhano umene anachititsa lero ku Mulanje.

21/07/2024



Full time

Karonga United 2 FCB Nyasa Big Bullets 1

MAFCO FC 0 Mighty Mukuru Wanderers 0

Mzuzu City Hammers 1 Chitipa United 0

Silver Strikers 1 FOMO FC 0

A polisi ku Rumphi amanga mayi wina pomuganizira kuti wakhala akuba pa malo ochilira a mayi pa chipatala chachikulu cha ...
21/07/2024

A polisi ku Rumphi amanga mayi wina pomuganizira kuti wakhala akuba pa malo ochilira a mayi pa chipatala chachikulu cha m'bomali.

Wachiwiri kwa mneneli wa polisi ya Rumphi Ethel Mithi wati mayiyu ndi Grace Chisambi wa m'mudzi mwa Scott mfumu yaikulu Mnthwalo ku Mzimba.

Iwo ati mayitu amatolera katundu osiyanasiyana ngati akuthandiza anthu akakhala kuti akufuna kukonza pa malowa kenako osawonekaso.

Iwo ati mayiyu akaonekera ku bwalo la milandu komwe akayankhe mlandu wakuba.

David Banda, yemwe mayi ake ndi katswiri woyimba Madonna, akuti tsopano wayamba kukhala yekha mumzinda wa New York ku Am...
21/07/2024

David Banda, yemwe mayi ake ndi katswiri woyimba Madonna, akuti tsopano wayamba kukhala yekha mumzinda wa New York ku Amerika.

Zina mwa nyuzipepala za mdzikolo zati David wachita ngakhale mayi ake ali nkuthekera komusungabe popeza ali ndalama kutapa kutaya.

David akuti akumaphunzitsa anthu kuyimba gitala kuti apeze ndalama zogulira zakudya komanso kusamala chibwezi chake Maria Atuesta wa zaka 21 ku Bronx.

Iye akuti anauza atolannkhani kuti sakufuna kukula ndi moyo odalira, ndipo palibe vuto ndi moyo omwe akukhalawo.

Madonna adamutenga David mdziko muno kukhala mwana wake ali ndi zaka ziwiri.

20/07/2024



Gulu la mbadwa zokhudzidwa zapempha anthu andale komanso nzika zadziko lino kuti zipewe kugwiritsa ntchito imfa ya yawachiwiri kwa mtsogoleri wakale wa dziko lino Dr Saulos Chilima powononga mbiri ya Boma la Tonse lomwe akutsogolera Dr. Lazarus Chakwera.

M'modzi mwa akuluakulu a gululi a Pastor Thoko Banda ati ndikulakwitsa kumapeza zofooka za Boma pa imfayi ati pofuna kukwaniritsa zokhumba zawo pa ndale pomwe akuti izi zili ndikuthekera kosokoneza chitetezo cha dziko lino.

Iwo akuyankhula izi pa msonkhano wa olemba nkhani omwe akuchititsa mu mzinda wa Lilongwe.

A Banda apempha kuti anthu akuyenera kudikira mwachidwi zotsatira za kafufuku yemwe anachitika pa imfayi kuti zotsatira zake zituluka zotani.

Police in Mwanza have arrested a 20-year-old man for being found in possession of a pangolin.Gabriel Lazalo was arrested...
20/07/2024

Police in Mwanza have arrested a 20-year-old man for being found in possession of a pangolin.

Gabriel Lazalo was arrested during the night of Thursday at Thambani Village in Traditional Authority Govati by police officers who were patrolling the area.

Mwanza Police Station public relations officer Hope Kasakula said Lazalo, along with other two suspects, looked nervous at the moment they saw the officers on patrol.

This alarmed the police leading to a chase and Lazalo was subsequently arrested while holding the live pangolin. The other two suspects managed to escape and are still on the run.

  Timapopa zimbudzi pamtengo wotchipa kwambiri  ,CALL 0999088085
20/07/2024


Timapopa zimbudzi pamtengo wotchipa kwambiri

,CALL 0999088085

Mtsikana mukumuona apayu  anasowa pa 6 July dzina lake ndi Florence Mwale amaphuzila pa Dowa secondary school walemba JC...
20/07/2024

Mtsikana mukumuona apayu anasowa pa 6 July dzina lake ndi Florence Mwale amaphuzila pa Dowa secondary school walemba JC amachokela ku Nambuma tayesetsa kusaka koma sakupezeka nde chonde ndipangileniko post anthu anuwa atithandize nkutheka amuonako pena pake

Mukamuona chonde kaneneni ku police imene muli nayo pafupi kapena imbani phone pama number awa 👇👇👇👇

0999222746 Father
+27734629692 Father
0992484870 Mom
0980284332 in-law husband to her sister
0990228867 Brother Phillip
0990003008 Brother Frank Whatsapp line

Alex chonde tithandizeni chonde 🙏

Ambuye akudalitseni kwambiri 🙏🙏❤️

Anthu asanu ndi m'modzi anjatidwa pogenda ma ofesi a nthambi yowona zolowa ndi zotulukaAnthu asanu ndi m’modzi (6) mu nz...
20/07/2024

Anthu asanu ndi m'modzi anjatidwa pogenda ma ofesi a nthambi yowona zolowa ndi zotuluka

Anthu asanu ndi m’modzi (6) mu nzinda wa Lilongwe, ali m’manja mwa apolisi poganizilidwa kuti anali m'gulu la omwe anagenda ma ofesi a nthambi yowona zolowa ndikutuluka m’dziko muno (DICS) pa nkhani ya ziphaso.

Anthu omwe akuyendetsa mwambo wa chikumbutso cha yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Saulos Chilima ap...
20/07/2024

Anthu omwe akuyendetsa mwambo wa chikumbutso cha yemwe anali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino Dr Saulos Chilima apempha anthu omwe atenge nawo gawo pa mwambowu kuti asalowetse ndale pa zoyankhula zawo.

Iwo ati kuchita izi kuthandizira kupereka ulemu kwa Dr Chilima.

Ku m'mawa kuno kwakonzedwa mwambo wa mapemphero omwe achitikire pa bwalo la za masewero la Nsipe.

Dr Chilima, pamodzi ndi anthu ena asanu ndi atatu adamwalira pa ngozi ya ndege yomwe idachitika mu nkhalango ya Chikangawa m'boma la Mzimba m'mwezi wa June.

20/07/2024

Ndayika Yehova patsogolo panga nthawi zonse. Popeza Iyeyo ali kudzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.
Masalimo 16:8

Malawi wanga daily verses 🇲🇼💟
Good Morning malawi 😍

M’modzi wa akulu-akulu achipani cha Democratic Progressive (DPP), Paul Gadama wati nzabodza kuti iye walandira ndalama k...
19/07/2024

M’modzi wa akulu-akulu achipani cha Democratic Progressive (DPP), Paul Gadama wati nzabodza kuti iye walandira ndalama kuchokera ku chipani china kuti akasokoneze tsogolo la chipani cha Democratic Progressive (DPP) m’chigawo chapakati.

Malingana ndi malipoti apa masamba a m’chezo, Gadama akuti wapatsidwa ndalama zankhani-nkhani pofuna kuti agule ma voti ku msonkhano waukulu wachipani cha DPP (delegates) kuti akamusankhe ngati wachiwiri kwa mtsogoleri.

Koma, Gadama wawuza Timveni Online kuti ili ndibodza lankukhuniza ndipo anthu asakhulupire izi, ponena kuti iye amachikonda chipani cha DPP.

"Anthu omwe akukamba nkhani zimene-zo akungondiopa chabe chifukwa akudziwa kuti sangakawine pa ine ku msonkhano waukulu," watero Gadama.

Chipani cha Democratic Progressive DPP chikhala ndi msonkhano wake waukulu mwezi wa mawa (August).

Komiti yaikulu ya chipani cha UTM ikuyembekezeka kukumana mumzinda wa Lilongwe lero.Mneneri wa chipanichi a Felix Njawal...
19/07/2024

Komiti yaikulu ya chipani cha UTM ikuyembekezeka kukumana mumzinda wa Lilongwe lero.

Mneneri wa chipanichi a Felix Njawala wati mwa zina mkumanowu ukambirana za tsiku ndi malo a convention komanso ganizo lochoka mu mgwirizano wa Tonse.

A Njawala afotokozanso kuti akuluakulu a chipanichi (a National Executive Committee) anapanga kale chiganizo chochoka mu mgwirizanowu panthawi yomwe ankakhuza imfa ya yemwe anali mtsogoleri wawo malemu a Saulos Chilima

Mkumanowu ukudzanso pomwe pakuoneka kuti atsogoleri ena achipanichi akumalankhula zosiyana zomwe zikudzetsa chikaiko pa umodzi wa chipanichi.

Lamulungu likudzali, UTM ikuyembekezekanso kuchititsa msonkhano wake wa ndale ku Nsipe m'boma la Ntcheu pokumbukiranso kuti patha masiku 40 a Chilima ndi anthu ena asanu ndi atatu atafa pa ngozi ya ndege.

Atsogoleri a Central Executive Committee ya UTM pomwe ankalengeza kuti chipanichi chatuluka mu mgwirizano wa Tonse.

28/05/2023

*NEWS UPDATE GROUP*

Government has stressed the importance of consulting the public on issues that affect the country.

Government through the ministry of Water and sanitation and ministry Information had a public engagement meeting in Blantyre, on access to clean and safe water.

Speaking at the event, Deputy Minister of Water and Sanitation Liana Kakhobwe Chapota stressed that public consultation is very crucial in as far as water and sanitation is concerned.

Minister of Information, Moses Kunkuyu said such engagements gives people an opportunity to appreciate what government is doing in various sectors.

"Today we gave an update to the people on what is happening in their waterboards in efforts to providing clean water. " said Kunkuyu

Senior Chief Kuntaja expressed his gratitude for being part of the public engagement as it gave him an understanding of the initiatives that the waterboards do to be able to provide water to the masses.

📝NEWS UPDATE

Address

Devil Street
Lilongwe

Alerts

Be the first to know and let us send you an email when Malawi wanga posts news and promotions. Your email address will not be used for any other purpose, and you can unsubscribe at any time.

Contact The Organization

Send a message to Malawi wanga:

Videos

Share



You may also like